1. Ndani akunga wanzeru? Ndani adziwa tanthauzo la mau? Nzeru ya munthu iwalitsa nkhope yace, kuduwa kwa nkhope yace ndi kusanduka.
2. Nditi, Sunga mau a mfumu, makamaka m'kulumbira Mulungu.
3. Usakangaze kumcokera; usaumirire kanthu koipa; pakuti iyeyo amacita comwe cimkonda.
4. Pakuti mau a mfumu ali ndi mphamvu; ndipo ndani anganene kwa iye, Kodi ucita ciani?
5. Wosunga cilamulo sadzadziwa kanthu koipa; ndipo mtima wa munthu wanzeru udziwa nyengo ndi maweruzo;