3. Cisoni ciposa kuseka; pakuti nkhope yakugwa ikonza mtima.
4. Mtima wa anzeru uli m'nyumba ya maliro; koma mtima wa zitsiru uli m'nyumba ya kuseka.
5. Kumva cidzudzulo ca anzeru kupambana kumva nyimbo ya zitsiru.
6. Pakuti kuseka kwa citsiru kunga minga irikutetheka pansi pa mphika; icinso ndi cabe.
7. Indetu nsautso iyarutsa wanzeru; ndi mtulo uipitsa mtima.
8. Citsiriziro ca kanthu ciposa ciyambi cace; wofatsa mtima apambana wodzikuza mtima.
9. Usakangaze mumtima mwako kukwiya; pakuti mkwiyo ugona m'cifuwa ca zitsiru.
10. Usanene, Kodi bwanji masiku akale anapambana ano? Pakuti sulikufunsa mwanzeru pamenepo.