1. Mbiri yabwino iposa zonunkhira zabwino; ndi tsiku lakumwalira liposa tsiku lakubadwa.
2. Kunka ku nyumba ya maliro kupambana kunka ku nyumba ya madyerero; pakuti kujako ndi matsiriziro a anthu onse; ndipo omwe ali ndi moyo adzakumbukirapo.
3. Cisoni ciposa kuseka; pakuti nkhope yakugwa ikonza mtima.
4. Mtima wa anzeru uli m'nyumba ya maliro; koma mtima wa zitsiru uli m'nyumba ya kuseka.
5. Kumva cidzudzulo ca anzeru kupambana kumva nyimbo ya zitsiru.