20. Pakuti ukondwerenji, mwananga, ndi mkazi waciwerewere,Ndi kufungatira cifuwa ca mkazi wacilendo?
21. Pakuti njira za munthu ziri pamaso pa Yehova,Asinkhasinkha za mayendedwe ace onse.
22. Zoipazacezacezidzagwira woipa;Adzamangidwa ndi zingwe za ucimo wace.
23. Adzafa posowa mwambo;Adzasocera popusa kwambiri.