7. Nzeru ipambana, tatenga nzeru;M'kutenga kwako konseko utenge luntha.
8. Uilemekeze, ndipo idzakukweza;Idzakutengera ulemu pamene uifungatira.
9. Idzaika cisada ca cisomo pamtu pako;Idzakupatsa korona wokongola.
10. Tamvera mwananga, nulandire mau anga;Ndipo zaka za moyo wako zidzacuruka.
11. Ndakuphunzitsa m'njira ya nzeru,Ndakuyendetsa m'mayendedwe olungama.