5. Tenga nzeru, tenga luntha;Usaiwale, usapatuke pa mau a m'kamwa mwanga;
6. Usasiye nzeru, ndipo Idzakusunga;Uikonde, idzakucinjiriza.
7. Nzeru ipambana, tatenga nzeru;M'kutenga kwako konseko utenge luntha.
8. Uilemekeze, ndipo idzakukweza;Idzakutengera ulemu pamene uifungatira.
9. Idzaika cisada ca cisomo pamtu pako;Idzakupatsa korona wokongola.
10. Tamvera mwananga, nulandire mau anga;Ndipo zaka za moyo wako zidzacuruka.
11. Ndakuphunzitsa m'njira ya nzeru,Ndakuyendetsa m'mayendedwe olungama.
12. Mapazi ako sadzaombana ulikuyenda;Ukathamanga, sudzapunthwa.
13. Gwira mwambo, osauleka;Uusunge; pakuti ndiwo moyo wako.
14. Usalowe m'mayendedwe ocimwa,Usayende m'njira ya oipa.