25. Abvala mphamvu ndi ulemu;Nangoseka nthawi ya m'tsogolo.
26. Atsegula pakamwa pace ndi nzeru,Ndipo cilangizo ca cifundo ciri pa lilime lace.
27. Ayang'anira mayendedwe a banja lace,Sadya zakudya za ulesi.
28. Anace adzanyamuka, nadzamucha wodala;Mwamuna wace namtama, nati,
29. Ana akazi ambiri anacita mwangwiro,Koma iwe uposa onsewo.
30. Kukongola kungonyenga, maonekedwe okoma ndi cabe;Koma mkazi woopa Yehova adzatamandidwa.
31. Mumpatse zipatso za manja ace; Ndi nchito zace zimtame kubwalo.