23. Mwamuna wace adziwika kubwalo,Pokhala pakati pa akuru a dziko.
24. Asoka maraya abafuta, nawagulitsa;Napereka mipango kwa wogulitsa malonda.
25. Abvala mphamvu ndi ulemu;Nangoseka nthawi ya m'tsogolo.
26. Atsegula pakamwa pace ndi nzeru,Ndipo cilangizo ca cifundo ciri pa lilime lace.
27. Ayang'anira mayendedwe a banja lace,Sadya zakudya za ulesi.
28. Anace adzanyamuka, nadzamucha wodala;Mwamuna wace namtama, nati,
29. Ana akazi ambiri anacita mwangwiro,Koma iwe uposa onsewo.