15. Aukanso kusanace,Napatsa banja lace zakudya, nagawira adzakazi ace nchito.
16. Asinkhasinkha za munda, naugula;Naoka mipesa ndi zipatso za manja ace.
17. Amanga m'cuuno mwace ndi mphamvu,Nalimbitsa mikono yace,
18. Azindikira kuti malonda ace ampindulira;Nyali yace sizima usiku.
19. Agwira njinga ya thonje ndi dzanja lace,Nafumbata mtengo wace.
20. Aolowera cikhato cace osauka;Natambasulira aumphawi manja ace.
21. Saopera banja lace cipale cofewa;Pakuti banja lace lonse libvala mlangali.
22. Adzipangira zimbwi zamaangamaanga;Nabvala bafuta ndi guta woti biriwiri.
23. Mwamuna wace adziwika kubwalo,Pokhala pakati pa akuru a dziko.
24. Asoka maraya abafuta, nawagulitsa;Napereka mipango kwa wogulitsa malonda.
25. Abvala mphamvu ndi ulemu;Nangoseka nthawi ya m'tsogolo.
26. Atsegula pakamwa pace ndi nzeru,Ndipo cilangizo ca cifundo ciri pa lilime lace.
27. Ayang'anira mayendedwe a banja lace,Sadya zakudya za ulesi.
28. Anace adzanyamuka, nadzamucha wodala;Mwamuna wace namtama, nati,
29. Ana akazi ambiri anacita mwangwiro,Koma iwe uposa onsewo.
30. Kukongola kungonyenga, maonekedwe okoma ndi cabe;Koma mkazi woopa Yehova adzatamandidwa.
31. Mumpatse zipatso za manja ace; Ndi nchito zace zimtame kubwalo.