10. Mkazi wangwiro ndani angampeze?Pakuti mtengo wace uposa ngale.
11. Mtima wa mwamuna wace umkhulupirira,Sadzasowa phindu.
12. Mkaziyo amcitira zabwino, si zoipa,Masiku onse a moyo wace.
13. Afuna ubweya ndi thonje,Nacita mofunitsa ndi manja ace.
14. Akunga zombo za malonda;Nakatenga zakudya zace kutari.
15. Aukanso kusanace,Napatsa banja lace zakudya, nagawira adzakazi ace nchito.
16. Asinkhasinkha za munda, naugula;Naoka mipesa ndi zipatso za manja ace.
17. Amanga m'cuuno mwace ndi mphamvu,Nalimbitsa mikono yace,