3. Mwamuna wokonda nzeru akondweretsa atate wace;Koma wotsagana ndi akazi adama amwaza cuma.
4. Mfumu akhazikitsa dziko ndi ciweruzo;Koma wosonkhetsa anthu mphatso alipululutsa.
5. Wosyasyalika mnzace Acherera mapazi ace ukonde.
6. M'kulakwa kwa woipa muli msampha;Koma wolungama ayimba, nakondwera.
7. Wolungama asamalira mlandu wa osauka;Koma woipa alibe nzeru yakuudziwa.
8. Anthu onyoza atentha mudzi;Koma anzeru alezetsa mkwiyo.
9. Munthu wanzeru akatsutsana ndi munthu wopusa,Ngakhale akwiya, ngakhale aseka, palibe mtendere.
10. Anthu ankhanza ada wangwiro;Koma oongoka mtima asamalira moyowace.
11. Citsiru cibvumbulutsa mkwiyo wace wonse;Koma wanzeru auletsa nautontholetsa.
12. Mkuru akamvera cinyengo,Atumuki ace onse ali oipa,
13. Waumphawi ndi wotsendereza akumana;Yehova apenyetsa maso a onse awiriwo.
14. Mfumu yolamulira osauka mwantheradi,Mpando wace udzakhazikika kufikira nthawi zonse.
15. Ntyole ndi cidzudzulo zipatsa nzeru;Koma mwana womlekerera acititsa amace manyazi.
16. Pocuruka oipa zolakwa zicuruka;Koma olungama adzaona kugwa kwao.
17. Langiza mwana wako, ndipo adzakupumitsa;Nadzasangalatsa moyo wako.
18. Popanda cibvumbulutso anthu amasauka;Koma wosunga cilamulo adalitsika.
19. Kapolo sangalangizidwe ndi mau,Pakuti azindikira koma osabvomera.
20. Kodi uona munthu wansontho m'mau ace?Ngakhale citsiru cidzacenjera, koma ameneyo ai.