23. Izinso ziri za anzeru.Poweruza cetera siliri labwino.
24. Wonenakwa woipa, Wolungama iwe;Magulu a anthu adzamtemberera, mitundu ya anthu idzamkwiyira,
25. Omwe amdzudzula adzasekera,Nadzadalitsika ndithu.
26. Wobwezera mau oongokaApsompsona milomo.
27. Longosola nchito yako panjapo, nuikonzeretu kumunda;Pambuyo pace ndi kumanga nyumba yako.
28. Usacitire mnzako umboni womtsutsa opanda cifukwa;Kodi udzanyenga ndi milomo yako?
29. Usanene, Ndidzamcitira zomwezo anandicitira ine;Ndidzabwereza munthuyo monga mwa macitidwe ace.
30. Ndinapita pa munda wa wolesi,Polima mphesa munthu wosowa nzeru.
31. Taonani, ponsepo panamera minga,Ndi kuwirirapo khwisa;Chinga lace lamiyala ndi kupasuka.