17. Mtima wako usacitire nsanje akucimwawo;Koma opabe Yehova tsiku lonse;
18. Pakutitu padzakhala mphotho;Ndipo ciyembekezo cako sicidzalephereka.
19. Tamvera tsopano, mwananga, utenge nzeru,Ulunjikitse mtima wako m'njiramo.
20. Usakhale mwa akumwaimwa vinyo,Ndi ankhuli osusuka.
21. Pakuti wakumwaimwa ndi wosusukayo adzasauka;Ndipo kusinza kudzabveka munthu nsanza.
22. Tamvera atate wako anakubala,Usapeputse amako atakalamba.
23. Gula ntheradi, osaigulitsa;Nzeru, ndi mwambo, ndi luntha.
24. Atate wa wolungama adzasekeradi;Wobala mwana wanzeru adzakondwera naye.