26. Ena asirira modukidwa tsiku lonse;Koma wolungama amapatsa osamana.
27. Nsembe ya oipa inyansa;Makamaka pakudza nayo iwo mwaciwembu.
28. Mboni yonama idzafa;Koma mwamuna wakumvetsa adzanena mosakayika,
29. Munthu woipa aumitsa nkhope yace;Koma woongoka mtima akonza njira zace.
30. Kulibe nzeru ngakhale lunthaNgakhale uphungu wotsutsana ndi Yehova.