1. Mtima wa mfumu uli m'dzanja la Yehova ngati mitsinje ya madzi;Aulozetsa komwe afuna.
2. Njira zonse za munthu zilungama pamaso pace;Koma Yehova ayesa mitima.
3. Kucita cilungamo ndi ciweruzoKupambana ndi nsembe kumkonda Yehova.
4. Maso akunyada, ndi mtima wodzikuza,Ndi nyali ya oipa, ziri cimo.
5. Zoganizira za wakhama zicurukitsadi katundu;Koma yense wansontho angopeza umphawi.
6. Kupata cuma ndi lilime lonama ndiko nkhungu yoyendayenda, ngakhale misampha ya imfa.
7. Ciwawa ca amphulupulu cidzawakokolola;Cifukwa akana kucita ciweruzo.