23. Miyeso yosiyana inyansa Yehova,Ndi mulingo wonyenga suli wabwino.
24. Yehova alongosola mayendedwe a mwamuna;Munthu tsono angazindikire bwanji njira yace?
25. Kunena mwansontho, ici ncopatulika, kuli msampha kwa munthu,Ndi kusinkhasinkha pambuyo pace atawinda.
26. Mfumu yanzeru ipeta amphulupulu,Niyendetsapo njinga ya gareta.