7. Njira za munthu zikakonda Yehova,Ayanjanitsana naye ngakhale adani ace.
8. Zapang'ono, pokhala cilungamo,Ziposa phindu lalikuru lopanda ciweruzo.
9. Mtima wa munthu ulingalira njira yace;Koma Yehova ayendetsa mapazi ace.
10. Mau a mlauli ali m'milomo ya mfumu;M'kamwa mwace simudzacita cetera poweruza.
11. Mwini muyeso ndi mulingo wolungama ndiye Yehova;Ndiyenso anapanga miyala yonse yoyesera ya m'thumba.
12. Kucita mphulupulu kunyansa mafumu;Pakuti mpando wao wakhazikika ndi cilungamo.
13. Milomo yolungama ikondweretsa mafumu;Wonena zoongoka amkonda.
14. Mkwiyo wa mfumu ndi mithenga ya imfa;Wanzeru adzaukhulula.
15. M'kuunika kwa nkhope ya mfumu muli moyo;Kukoma mtima kwace kunga mtambo wa mvula ya masika.
16. Kodi kulandira nzeru sikupambana ndi golidi,Kulandira luntha ndi kusankhika koposa siliva?
17. Khwalala la oongoka mtima ndilo lakuti asiye zoipa;Wosunga njira yace acinjiriza moyo wace.
18. Kunyada kutsogolera kuonongekaMtinia wodzikuza ndi kutsogolera kupunthwa.
19. Kufatsa mtima ndi osaukaKuposa kugawana zofunkha ndi onyada.
20. Wolabadira mau adzapeza bwino;Ndipo wokhulupirira Yehova adala.