6. Mphulupulu iomboledwa ndi cifundo ndi ntheradi;Apatuka pa zoipa poopa Yehova.
7. Njira za munthu zikakonda Yehova,Ayanjanitsana naye ngakhale adani ace.
8. Zapang'ono, pokhala cilungamo,Ziposa phindu lalikuru lopanda ciweruzo.
9. Mtima wa munthu ulingalira njira yace;Koma Yehova ayendetsa mapazi ace.
10. Mau a mlauli ali m'milomo ya mfumu;M'kamwa mwace simudzacita cetera poweruza.
11. Mwini muyeso ndi mulingo wolungama ndiye Yehova;Ndiyenso anapanga miyala yonse yoyesera ya m'thumba.
12. Kucita mphulupulu kunyansa mafumu;Pakuti mpando wao wakhazikika ndi cilungamo.