24. Mau okoma ndiwo cisa ca uci,Otsekemera m'moyo ndi olamitsa mafupa.
25. Iripo njira yooneka kwa mwamuna ngati yoongoka,Koma matsiriziro ace ndi njira za imfa.
26. Wanchito adzigwirira yekha nchito;Pakuti m'kamwa mwace mumfulumiza.
27. Munthu wopanda pace akonzeratu zoipa;Ndipo m'milomo mwace muli moto wopsereza.
28. Munthu wokhota amautsa makani;Kazitape afetsa ubwenzi.
29. Munthu waciwawa akopa mnzace,Namuyendetsa m'njira yosakhala bwino.
30. Wotsinzina ndiye aganizira zakhota;Wosunama afikitsa zoipa.
31. Imvi ndiyo korona wa ulemu,Idzapezedwa m'njira ya cilungamo.
32. Wosakwiya msanga aposa wamphamvu;Wolamulira mtima wace naposa wolanda mudzi.
33. Maere aponyedwa pamfunga;Koma ndiye Yehova alongosola zonse.