2. Cuma ca ucimo sicithangata:Koma cilungamo cipulumutsa kuimfa.
3. Yehova samvetsa njala moyo wa wolungama;Koma amainga cifuniro ca wocimwa.
4. Wocita ndi dzanja laulesi amasauka;Koma dzanja la akhama lilemeretsa.
5. Wokolola m'malimwe ndi mwana wanzeru;Koma wogona pakututa ndi mwana wocititsa manyazi.
6. Madalitso ali pamtu pa wolungamaKoma m'kamwa mwa oipa mubisa ciwawa.
7. Amayesa wolungama wodala pamkumbukira;Koma dzina la oipa lidzabvunda.
8. Mwini mtima wanzeru amalandira malamulo;Koma citsiru colongolola cidzagwa.
9. Woyenda moongoka amayenda osatekeseka;Koma wokhotetsa njira zace adzadziwika.
10. Wotsinzinira acititsa cisoni;Koma wodzudzula momveka acita mtendere.
11. M'kamwa mwa wolungama ndi kasupe wa moyo;Koma m'kamwa mwa oipa mubisa ciwawa.
12. Udani upikisanitsa;Koma cikondi cikwirira zolakwa zonse.
13. Nzeru ipezedwa m'milomo ya wozindikira;Koma wopusa pamsana pace ntyole.
14. Anzeru akundika zomwe adziwaKoma m'kamwa mwa citsiru muononga tsopano lino.
15. Cuma ca wolemera ndi mudzi wace wolimba;Koma umphawi wao uononga osauka.
16. Nchito za wolungama zipatsa moyo;Koma phindu la oipa licimwitsa.