1. Yehova acita ufumu; dziko lapansi likondwere;Zisumbu zambiri zikondwerere.
2. Pomzinga pali mitambo ndi mdima;Cilungamo ndi ciweruzo ndizo zolimbitsa mpando wacifumu wace.
3. Moto umtsogolera,Nupsereza otsutsana naye pozungulirapo,
4. Mphezi zace zinaunikira dziko lokhalamo anthu;Dziko lapansi linaona nilinagwedezeka.
5. Mapiri anasungunuka ngati sera pamaso pa Yehova,Pamaso pa Ambuye wa dziko lonse lapansi.