3. Mundicitire cifundo, Ambuye;Pakuti tsiku lonse ndiitana Inu.
4. Kondwetsani moyo wa mtumiki wanu;Pakuti ndikwezera moyo wanga kwa Inu, Ambuye.
5. Pakuti fnu, Ambuye, ndinu wabwino, ndi wokhululukira,Ndi wa cifundo cocurukira onse akuitana Inu.
6. Cherani khutu pemphero langa, Yehova;Nimumvere mau a kupemba kwanga,
7. Tsiku la msauko wanga ndidzaitana Inu;Popeza mudzandibvomereza.
8. Pakati pa milungu palibe wina wonga Inu, Ambuye;Ndipo palibe nchito zonga zanu.