1. Cherani khutu lanu Yehova, mundiyankhe;Pakuti ine ndine wozunzika ndi waumphawi.
2. Sungani moyo wanga pakuti ine ndine wokondedwa wanu;Inu Mulungu wanga, pulumutsani mtumiki wanu wokhulupirira Inu.
3. Mundicitire cifundo, Ambuye;Pakuti tsiku lonse ndiitana Inu.
4. Kondwetsani moyo wa mtumiki wanu;Pakuti ndikwezera moyo wanga kwa Inu, Ambuye.
5. Pakuti fnu, Ambuye, ndinu wabwino, ndi wokhululukira,Ndi wa cifundo cocurukira onse akuitana Inu.
6. Cherani khutu pemphero langa, Yehova;Nimumvere mau a kupemba kwanga,