1. Cherani khutu lanu Yehova, mundiyankhe;Pakuti ine ndine wozunzika ndi waumphawi.
2. Sungani moyo wanga pakuti ine ndine wokondedwa wanu;Inu Mulungu wanga, pulumutsani mtumiki wanu wokhulupirira Inu.
3. Mundicitire cifundo, Ambuye;Pakuti tsiku lonse ndiitana Inu.