7. Mulungu wa makamu, mutibweze;Nimuwalitse nkhope yanu, ndipo tidzapulumuka.
8. Mudatenga mpesa kucokera ku Aigupto:Munapitikitsa amitundu ndi kuuoka uwu.
9. Mudasoseratu pookapo,Idagwiritsa mizu yace, ndipo unadzaza dziko.
10. Mthunzi wace unaphimba mapiri,Ndi nthambi zace zikunga mikungudza ya Mulungu.