69. Ndipo anamanga malo oyera ace ngati kaphiri,Monga dziko lapansi limene analikhazikitsa kosatha.
70. Ndipo anasankha Davide mtumiki wace,Namtenga ku makola a nkhosa:
71. Anamtenga kuja anatsata zoyamwitsa,Awete Yakobo, anthu ace, ndi Israyeli, colandira cace.