66. Ndipo anapanda otsutsana naye kumbuyo;Nawapereka akhale otonzeka kosatha.
67. Tero anakana hema wa Yosefe;Ndipo sanasankha pfuko la Efraimu;
68. Koma anasankha pfuko la Yuda,Phiri la Ziyoni limene analikonda.
69. Ndipo anamanga malo oyera ace ngati kaphiri,Monga dziko lapansi limene analikhazikitsa kosatha.
70. Ndipo anasankha Davide mtumiki wace,Namtenga ku makola a nkhosa:
71. Anamtenga kuja anatsata zoyamwitsa,Awete Yakobo, anthu ace, ndi Israyeli, colandira cace.
72. Potero anawaweta monga mwa mtima wace wangwiro;Nawatsogolera ndi luso la manja ace.