55. Ndipo anapitikitsa amitundu pamaso pao,Nawagawira colowa cao, ndi muyeso,Nakhalitsa mafuko a Israyeli m'mahema mwao.
56. Koma anamuyesa napikisana ndi Mulungu Wam'mwambamwamba,Osasunga mboni zace;
57. Koma anabwerera m'mbuyo, nacita zosakhulupirika monga makolo ao:Anapatuka ngati uta wolenda,
58. Ndipo anautsa mtima wace ndi malo amsanje ao,Namcititsa nsanje ndi mafano osema.
59. Pakumva ici Mulungu, anakwiya, Nanyozatu Israyeli;
60. Ndipo anacokera cokhalamo ca ku Silo,Cihemaco adacimanga mwa anthu;
61. Napereka mphamvu yace m'ukapolo,Ndi ulemerero wace m'dzanja la msautsi.
62. Naperekanso anthu ace kwa lupanga;Nakwiya naco colandira cace.
63. Moto unapsereza anyamata ao;Ndi anamwali ao sanalemekezeka.
64. Ansembe ao anagwa ndi lupanga;Ndipo amasiye ao sanacita maliro.
65. Pamenepo Ambuye anauka ngati wam'tulo;Ngati ciphona cakucita nthungululu ndi vinyo.
66. Ndipo anapanda otsutsana naye kumbuyo;Nawapereka akhale otonzeka kosatha.