42. Sanakumbukila dzanja lace,Tsikuli anawaombola kwa msautsi.
43. Amene anaika zizindikilo zace m'Aigupto,Ndi zodabwiza zace ku cidikha ca Zoanu;
44. Nasanduliza nyanja yao mwazi,Ndi mitsinje yao, kuti sangakhoze kumwa.
45. Anawatumizira pakati pao mitambo ya nchenche zakuwatha;Ndi acule akuwaononga.
46. Ndipo anapatsa mphuci dzinthu dzao,Ndi dzombe nchito yao.