30. Asanathe naco cokhumba cao,Cakudya cao ciri m'kamwa mwao,
31. Pamenepo mkwiyo wa Mulungu unawaukira,Ndipo anapha mwa onenepa ao,Nagwetsa osankhika a Israyeli.
32. Cingakhale ici conse anacimwanso,Osabvomereza zodabwiza zace.
33. Potero anathera masiku ao ndi zopanda pace,Ndi zaka zao mwa mantha.
34. Pamene anawapha ndipo anamfuna Iye;Nabwerera, nafunitsitsa Mulungu,
35. Ndipo anakumbukila kuti Mulungu ndiye thanthwe lao,Ndi Mulungu Wam'mwambamwamba Mombolo wao.