21. Cifukwa cace Yehova anamva, nakwiya;Ndipo anayatsa moto pa Yakobo,Ndiponso mkwiyo unakwera pa Israyeli;
22. Popeza sanakhulupirira Mulungu,Osatama cipulumutso cace.
23. Koma analamulira mitambo iri m'mwamba,Natsegula m'makomo a kumwamba.
24. Ndipo anawabvumbitsira mana, adye,Nawapatsa tirigu wa kumwamba.
25. Yense anadya mkate wa omveka:Anawatumizira cakudya cofikira,
26. Anaombetsa m'mwamba mphepo ya kum'mawa:Natsogoza mwela ndi mphamvu yace.
27. Ndipo anawabvumbitsira nyama ngati pfumbi,Ndi mbalame zouluka ngati mcenga wa kunyanja:
28. Ndipo anazigwetsa pakati pa misasa yao,Pozungulira pokhala iwo.
29. Potero anadya nakhuta kwambiri;Ndipo anawapatsa cokhumba iwo.
30. Asanathe naco cokhumba cao,Cakudya cao ciri m'kamwa mwao,