13. Mudagawa nyanja ndi mphamvu yanu;Mudaswa mitu ya zoopsa za m'madzi.
14. Mudaphwanya mitu ya livyatanu;Mudampereka akhale cakudya ca iwo a m'cipululu.
15. Mudagawa kasupe ndi mtsinje;Mudaphwetsa mitsinje yaikuru.
16. Usana ndi wanu, usikunso ndi wanu:Munakonza kuunika ndi dzuwa.
17. Munaika malekezero onse a dziko lapansi;Munalenga dzinja ndi malimwe.
18. Mukumbukile ici, Yehova, mdaniyo anatonza,Ndipo anthu opusa ananyoza dzina lanu.