22. Ndiponso ndidzakuyamikani ndi cisakasa,Kubukitsa coonadi canu, Mulungu wanga;Ndidzakuyimbirani Nyimbo ndi zeze,Ndinu Woyerayo wa Israyeli.
23. Milomo yanga idzapfuula mokondwera poyimbira Inu Nyimbo;Inde, moyo wanga umene munaombola.
24. Lilime langa lomwe lidzalankhula za cilungamo canu tsiku lonse:Pakuti ofuna kundicitira coipa acita manyazi, nadodoma.