1. Ndikhulupirira Inu, Yehova:Ndisacite manyazi nthawi zonse.
2. Ndikwatuleni m'cilungamo canu, ndi kundilanditsa:Ndicherereni khutu lanu ndi kundipulumutsa.
3. Mundikhalire thanthwe lokhalamo, lopitako kosaleka;Mwalamulira kundipulumutsa;Popeza Inu ndinu thanthwe langa ndi linga langa,
4. Ndilanditseni, Mulungu wanga, m'dzanja la woipa,M'dzanja la munthu wosalungama ndi waciwawa.
5. Pakuti Inu ndinu ciyembekezo canga, Ambuye Yehova;Mwandikhalira wokhulupirika kuyambira ubwana wanga.
6. Inu munandigwirizizakuyambira ndisanabadwe:Kuyambira pa thupi la mai wanga wondicitira zokoma ndinu;Ndidzakulemekezani kosalekeza.
7. Ndikhala codabwiza kwa ambiri;Koma Inu ndinu pothawira panga polimba.
8. M'kamwa mwanga mudzadzala lemekezo lanu,Ndi ulemu wanu tsiku lonse.
9. Musanditaye mu ukalamba wanga;Musandisiye, pakutha mphamvu yanga.
10. Pakuti adani anga alankhula za ine;Ndipo iwo akulalira moyo wanga apangana upo,