1. Mwatitaya Mulungu, mwatipasula;Mwakwiya; tibwezereni.
2. Mwagwedeza dziko, mwaling'amba:Konzani ming'alu yace; pakuti ligwedezeka.
3. Mwaonetsa anthu anu zowawa:Mwatimwetsa vinyo wotinjenjemeretsa.
4. Koma mwapatsa mbendera akuopa Inu,Aikweze cifukwa ca coonadi.
5. Kuti okondedwa anu alanditsidwe,Pulumutsani ndi dzanja lanu lamanja, ndipo mutibvomereze.