1. Mwatitaya Mulungu, mwatipasula;Mwakwiya; tibwezereni.
2. Mwagwedeza dziko, mwaling'amba:Konzani ming'alu yace; pakuti ligwedezeka.
3. Mwaonetsa anthu anu zowawa:Mwatimwetsa vinyo wotinjenjemeretsa.
4. Koma mwapatsa mbendera akuopa Inu,Aikweze cifukwa ca coonadi.
5. Kuti okondedwa anu alanditsidwe,Pulumutsani ndi dzanja lanu lamanja, ndipo mutibvomereze.
6. Mulungu walankhula m'ciyero cace; ndidzakondwerera:Ndidzagawa Sekemu, ndidzayesa muyeso cigwa ca Sukoti.
7. Gileadi ndi wanga, Manasenso ndi wanga;Ndipo Efraimu ndi mphamvu ya mutu wanga;Yuda ndiye wolamulira wanga,
8. Moabu ndiye mkhate wanga;Pa Edomu ndidzaponya nsapato yanga:Filistiya, pfuulatu cifukwa ca ine.
9. Adzandifikitsa ndani m'mudzi wa m'linga?Adzanditsogolera ndani ku Edomu?
10. Si ndinu, Mulungu, amene mwantaya?Osaturuka nao makamu athu, Mulungu.
11. Tithandizeni kunsautso;Kuti cipulumutso ca munthu ndi cabe.