4. Osawapatsa cifukwa ine, athamanga nadzikonza;Galamukani kukomana nane, ndipo penyani.
5. Ndinu Yehova, Mulungu wa makamu, Mulungu wa Israyeli,Ukani kukazonda amitundu onse:Musacitire cifundo mmodzi yense wakucita zopanda pace monyenga.
6. Abwera madzulo, auwa ngati garu,Nazungulira mudzi.
7. Onani abwetuka pakamwa pao;M'milomo mwao muli lupanga,Pakuti amati, Amva ndani?
8. Koma Inu, Yehova, mudzawaseka;Mudzalalatira amitundu onse.
9. Inu, mphamvu yanga, ndidzakulindirani;Pakuti Mulungu ndiye msanje wanga.
10. Mulungu wa cifundo canga adzandikumika:Adzandionetsa tsoka la adani anga.
11. Musawapheretu, angaiwale anthu anga:Muwabalalitse mwa mphamvu yanu, ndipo muwagwetse,Ambuye, ndinu cikopa cathu.
12. Pakamwa pao acimwa ndi mau onse a pa milomo yao,Potero akodwe m'kudzitamandira kwao,Ndiponso cifukwa ca kutemberera ndi bodza azilankhula.
13. Muwathe mumkwiyo, muwagurule psiti:Ndipo adziwe kuti Mulungu ndiye woweruza m'Yakobo,Kufikira malekezero a dziko la pansi.
14. Ndipo abwere madzulo, auwe ngati garu,Nazungulire mudzi.
15. Ayendeyende ndi kufuna cakudya,Nacezere osakhuta.