6. Anandichera ukonde apo ndiyenda;Moyo wanga wawerama:Anandikumbira mbuna patsogolo panga;Anagwa m'kati mwace iwo okha.
7. Mtima wanga wakhazikika, Mulungu, ndakhazika mtima;Ndidzayimba, inde, ndidzayimba zolemekeza.
8. Galamuka, ulemu wanga; galamukani cisakasa ndi zeze:Ndidzauka ndekha mamawa.
9. Ndidzakuyamikirani mwa anthu, Ambuye:Ndidzakuyimbirani mwa mitundu.
10. Pakuti cifundo canu ncacikuru kufikira m'mwamba,Ndi coonadi canu kufikira mitambo.
11. Kwezekani m'mwambamwamba, Mulungu;Ulemerero wanu ukhale pamwamba m'dziko lonse lapansi.