4. Pakuti Inu sindinu Mulungu wakukondwera naco coipaMphulupulu siikhala ndi Inu.
5. Opusa sadzakhazikika pamaso panu:Mudana nao onse akucita zopanda pace.
6. Mudzaononga iwo akunena bodza:Munthu wokhetsa mwazi ndi wacinyengo, Yehova anyansidwa naye.
7. Koma ine, mwa kucuruka kwa cifundo canu ndidzalowa m'nyumba yanu:Ndidzagwada kuyang'ana Kacisi wanu woyera ndi kuopa Inu.
8. Yehova, munditsogolere m'cilungamo canu, cifukwa ca akundizondawo;Mulungamitse njira yanu pamaso panga.