10. Muwayese otsutsika Mulungu;Agwe nao uphungu wao:M'kucuruka kwa zolakwa zao muwapitikitse;Pakuti anapikisana ndi Inu.
11. Koma akondwere onse amene athawira kwa Inu,Apfuule mokondwera kosaleka, popeza muwafungatira;Nasekere mwa Inu iwo akukonda dzina lanu.
12. Pakuti Inu, Yehova, mudzadalitsa wolungamayo;Mudzamcinjiriza naco cibvomerezo ngati cikopa.