9. Tidalingalira za cifundo canu, Mulungu,M'kati mwa Kacisi wanu.
10. Monga dzina lanu, Mulungu,Momwemo lemekezo lanu ku malekezero a dziko lapansi:M'dzanja lamanja lanu mudzala cilungamo.
11. Likondwere phiri la Ziyoni,Asekere ana akazi a Yuda,Cifukwa ca maweruzo anu.
12. Zungulirani Ziyoni, ndipo muuzinge;Werengani nsanja zace.
13. Penyetsetsani malinga ace,Yesetsani zinyumba zace;Kuti mukaziwerengere mibadwo ikudza m'mbuyo.
14. Pakuti Mulungu ameneyo ndiye Mulungu wathu ku nthawi za nthawi:Adzatitsogolera kufikira imfa.