1. Yehova ndiye wamkulu, ayenera kulemekezekadi,M'mudzi wa Mulungu wathu, m'phiri lace loyera.
2. Phiri la Ziyoni, cikhalidwe cace ncokomaKu mbali zace za kumpoto,Ndilo cimwemwe ca dziko lonse lapansi,Mudzi wa mfumu yaikuru.
3. Mulungu adziwika m'zinyumba zace ngati msanje.
4. Pakuti, taonani, mafumuwo anasonkhana,Anapitira pamodzi.
5. Anapenya mudziwo, ndipo pamenepo anadabwa;Anaopsedwa, nathawako.