8. Adzakhuta kwambiri ndi zonona za m'nyumba mwanu:Ndipo mudzawamwetsa mu mtsinje wa zokondweretsa zanu.
9. Pakuti citsime ca moyo ciri ndi Inu:M'kuunika kwanu tidzaona kuunika.
10. Tanimphitsani cifundo canu pa iwo akudziwa Inu;Ndi cilungamo canu pa oongoka mtima.
11. Phazi la akudzikuza lisandifikire ine,Ndi dzanja la oipa lisandicotse.
12. Pomwepo padagwera ocita zopanda pace:Anawalikha, ndipo sadzatha kuukanso.