8. Ine ndidzakulangiza ndi kuphunzitsa iwe za njira ukayendayo;Ndidzakupangira ndi diso langa lakuyang'ana iwe.
9. Musakhale monga kavalo, kapena ngati buru, wopanda nzeru:Zomangira zao ndizo cam'kamwa ndi capamutu zakuwakokera,Pakuti ukapanda kutero sadzakuyandikiza.
10. Zisoni zambiri zigwera woipa:Koma cifundo cidzamzinga iye wakukhulupirira Yehova.
11. Sekerani mwa Yehova, ndimo kondwerani inu olungama mtima;Ndipo pfuulani mokondwera nonsenu oongoka mtima.