8. Yehova, ndikonda cikhalidwe ca nyumba yanu,Ndi malo akukhalamo ulemerero wanu.
9. Musandicotsere mzimu wanga pamodzi ndi olakwa,Kapena moyo wanga pamodzi ndi anthu okhetsa mwazi:
10. Amene m'manja mwao muli mphulupulu,Ndi dzanja lao lamanja ladzala ndi zokometsera mlandu.
11. Koma ine, ndidzayenda m'ungwiro wanga;Mundiombole, ndipo ndicitireni cifundo.
12. Phazi langa liponda pacidikha:M'masonkhano ndidzalemekeza Yehova.