34. Aphunzitsa manja anga agwire nkhondo;Kuti walifuka uta wamkuwa ndi manja anga.
35. Ndipo mwandipatsa cikopa ca cipulumutso canu:Ndipo dzanja lamanja lanu landigwiriziza,Ndipo cifatso canu candikuza ine.
36. Mwandipondetsa patali patali,Sanaterereka mapazi anga.
37. Ndidzalondola adani anga, ndi kuwapeza:Ndipo sindidzabwerera asanathe psiti.
38. Ndidzawapyoza kuti sangakhoze kuuka:Adzagwa pansi pa mapazi anga,