1. Ndidzakuyamikani ndi mtima wangawonse;Ndidzayimba zakukulemekezani patsogolo pa milungu,
2. Ndidzagwadira kuloza ku Kacisi wanu woyera,Ndi kuyamika dzina lanu,Cifukwa ca cifundo canu ndi coonadi canu;Popeza munakuzitsa mau anu koposa dzina lanu lonse.
3. Tsiku loitana ine, munandiyankha,Munandilimbitsa ndi mphamvu m'moyo mwanga.
4. Mafumu onse a pa dziko lapansi adzakuyamikani,Yehova, popeza adamva mau a pakamwa panu.
5. Ndipo adzayimbira njira za Yehova;Pakuti ulemerero wa Yehova ndi waukuru.
6. Angakhale Yehova ngwokwezeka, apenyanso wopepukayo;Koma wodzikuza amdziwira kutali.
7. Ndingakhale ndiyenda pakati pa nsautso, mudzandipatsa moyo;Mudzatambasula dzanja lanu pa mkwiyo wa adani anu,Ndipo dzanja lanu lamanja lidzandipulumutsa.