13. Dzina lanu, Yehova, likhala kosatha;Cikumbukilo canu, Yehova, kufikira mibadwo mibadwo.
14. Pakuti Yehova adzaweruza anthu ace,Koma adzaleka atumiki ace.
15. Mafano a amitundu ndiwo siliva ndi golidi,Nchito ya manja a anthu.
16. Pakamwa ali napo koma osalankhula;Maso ali nao, koma osapenya;
17. Makutu ali nao, koma osamva;Inde, pakamwa pao palibe mpweya.
18. Akuwapanga adzafanana nao;Inde, onse akuwakhulupirira.
19. A nyumba ya Israyeli inu, lemekezani Yehova:A nyumba ya Aroni inu, lemekezani Yehova:
20. A nyumba ya Levi inu, lemekezani Yehova:Inu akuopa Yehova, lemekezani Yehova.
21. Alemekezedwe Yehova kucokera m'Ziyoni,Amene akhala m'Yerusalemu.Haleluya,