91. Kunena za maweruzo anu alimbikira kufikira lero;Pakuti onsewa ndiwo atumiki anu.
92. Cilamulo canu cikadapanda kukhala cikondweretso canga,Ndikadatayika m'kuzunzika kwanga.
93. Sindidzaiwala malangizo anu nthawi zonse;Popeza munandipatsa nao moyo.
94. Ine ndine wanu, ndipulumutseniPakuti ndinafuna malangizo anu.
95. Oipa anandilalira kundiononga;Koma ndizindikira mboni zanu.
96. Ndinapenya malekezero ace a ungwiro wonse;Koma lamulo lanu ndi lotakasuka ndithu.
97. Ha! Ndikondadi cilamulo canu;Ndilingiriramo ine tsiku lonse.
98. Malamulo anu andipatsa nzeru yakuposa adani anga;Pakuti akhala nane cikhalire.
99. Ndiri nayo nzeru yakuposa aphunzitsi anga onse;Pakuti ndilingalira mboni zanu.
100. Ndizindikira koposa okalambaPopeza ndinasunga malangizo anu.
101. Ndinaletsa mapazi anga njira iri yonse yoipa,Kuti ndisamalire mau anu.
102. Sindinapatukana nao maweruzo anu;Pakuti Inu munandiphunzitsa.