88. Mundipatse moyo monga mwa cifundo canu;Ndipo ndidzasamalira mboni ya pakamwa panu,
89. Mau anu aikika kumwamba,Kosatha, Yehova.
90. Cikhulupiriko canu cifikira mibadwo mibadwo;Munakhazikitsa dziko lapansi, ndipo likhalitsa.
91. Kunena za maweruzo anu alimbikira kufikira lero;Pakuti onsewa ndiwo atumiki anu.
92. Cilamulo canu cikadapanda kukhala cikondweretso canga,Ndikadatayika m'kuzunzika kwanga.
93. Sindidzaiwala malangizo anu nthawi zonse;Popeza munandipatsa nao moyo.
94. Ine ndine wanu, ndipulumutseniPakuti ndinafuna malangizo anu.
95. Oipa anandilalira kundiononga;Koma ndizindikira mboni zanu.
96. Ndinapenya malekezero ace a ungwiro wonse;Koma lamulo lanu ndi lotakasuka ndithu.
97. Ha! Ndikondadi cilamulo canu;Ndilingiriramo ine tsiku lonse.
98. Malamulo anu andipatsa nzeru yakuposa adani anga;Pakuti akhala nane cikhalire.
99. Ndiri nayo nzeru yakuposa aphunzitsi anga onse;Pakuti ndilingalira mboni zanu.